Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 1:32-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. koma Aseri anakhala pakati pa Akanani nzika za kudziko; pakuti sanawaingitsa.

33. Nafitali sanaingitsa nzika za ku Beti-semesi, kapena nzika za ku Beri-anati; koma anakhala pakati pa Akanani, nzika za kudziko; koma nzika za ku Beti-semesi, ndi a ku Beti-anati zinawasonkhera.

34. Ndipo Aamori anakankha ana a Dani akhale kumapiri pakuti sanawalola atsikire kucigwa;

35. Aamori anakhumbanso kukhala ku phiri la Heresi, ku Ajaloni, ndi ku Saalibimu; koma dzanja la a m'nyumba ya Yosefe linawalaka, nakhala iwo akupereka msonkho.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 1