Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Obadiya 1:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. MASOMPHENYA a Obadiya. Atero Ambuye Yehova za Edomu: Tamva mbiri yocokera kwa Yehova, ndi mthenga wotumidwa mwa amitundu, ndi kuti, Nyamukani, timuukire kumthira nkhondo.

2. Taona, ndakuika wamng'ono mwa amitundu; unyozedwa kwambiri.

3. Kudzikuza kwa mtima wako kwakunyenga, iwe wokhala m'mapanga a thanthwe, iwe pokhala pako pamwamba, wakunena m'mtima mwace, Adzanditsitsira pansi ndani?

4. Cinkana ukwera pamwamba peni peni ngati ciombankhanga, cinkana cisanja cako cisanjika pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa kumeneko, ati Yehova.

5. Akakudzera akuba, kapena mbala usiku, (Ha! waonongeka) sadzaba mpaka adzakhuta kodi? Akakudzera akuchera mphesa sadzasiya khunkha kodi?

Werengani mutu wathunthu Obadiya 1