Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nyimbo 7:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Mutu wako ukunga Karimeli,Ndi tsitsi la pamtu pako likunga nsaru yakuda;Mfumu yamangidwa ndi nkhata zace ngati wamsinga.

6. Ha, ndiwe wokongola ndi wofunika,Bwenziwe, m'zokondweretsa!

7. Msinkhu wakowu ukunga mlaza,Maere ako akunga matsango amphesa,

8. Ndinati, Ndikakwera pamlazapo,Ndikagwira nthambi zace:Maere ako ange ngati matsango amphesa,Ndi kununkhira kwa mpweya wako ngati maula;

9. M'kamwa mwako munge ngati vinyo woposa,Womeza tseketeke bwenzi langa,Wolankhulitsa milomo ya ogona tulo.

10. Ndine wa wokondedwa wanga mnyamatayo,Ndine amene andifunayo.

Werengani mutu wathunthu Nyimbo 7