Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nyimbo 5:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji,Mkaziwe woposa kukongola?Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji,Kuti utilumbirira motero?

10. Wokondedwa wanga ali woyera ndi wofiira,Womveka mwa zikwi khumi.

11. Mutu wace ukunga golidi, woyengetsa,Tsitsi lace lopotana, ndi lakuda ngati khungubwi.

12. Ana a maso ace akunga nkhunda pambali pa mitsinje ya madzi;Otsukidwa ndi mkaka, okhala pa mitsinje yodzala.

13. Masaya ace akunga citipula cabzyalamo ndiwo,Ngati mitumbira yoyangapo masamba onunkhira:Milomo yace ikunga akakombo, pakukhapo madzi a nipa.

Werengani mutu wathunthu Nyimbo 5