Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nyimbo 5:3-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndinayankha kuti, Ndabvula maraya anga, ndiwabvalenso bwanji?Ndatsuka mapazi anga; ndiwadetserenii?

4. Bwenzi langa analonga dzanja lace pazenera,Mtima wanga ndi kuguguda cifukwa ca iye,

5. Ndinauka ndikatsegulire bwenzi langa;Pamanja panga panakha nipa.Ndi pa zala zanga madzi a nipa, Pa zogwirira za mpikizo,

6. Ndinamtsegulira bwenzi langalo;Koma ndinampeza, bwenzi langa atacoka.Moyo wanga unalefuka polankhula iye:Ndinamfunafuna, osampeza;Ndinamuitana, koma sanandibvomera.

7. Alonda akuyenda m'mudzi anandipeza,Nandikantha, nanditema;Osunga maguta nandicotsera cophimba canga.

8. Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,Mukapeza bwenzi langa, mudzamuuza ciani?Kuti ndadwala ndi cikondi.

9. Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji,Mkaziwe woposa kukongola?Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji,Kuti utilumbirira motero?

10. Wokondedwa wanga ali woyera ndi wofiira,Womveka mwa zikwi khumi.

11. Mutu wace ukunga golidi, woyengetsa,Tsitsi lace lopotana, ndi lakuda ngati khungubwi.

12. Ana a maso ace akunga nkhunda pambali pa mitsinje ya madzi;Otsukidwa ndi mkaka, okhala pa mitsinje yodzala.

Werengani mutu wathunthu Nyimbo 5