Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nyimbo 2:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Dzanja lace lamanzere anditsamiritse kumutu,Dzanja lace lamanja ndi kundifungatira.

7. Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,Pali mphoyo, ndi nswala za kuthengo,Kuti musautse, ngakhale kugalamutsa cikondi,Mpaka cikafuna mwini.

8. Mau a wokondedwa wanga mnyamatayo! Taona, adza,Alikulumpha pamapiri, alikujidimuka pazitunda.

9. Wokondedwa wanga akunga mphoyo, pena mwana wa mbawala:Taona, aima patseri pa khoma pathu,Apenyera pazenera, Nasuzumira pamade.

10. Wokondedwa wanga analankhula, nati kwa ine,Tauka, bwenzi langa, wokongola wanga, tiye.

11. Pakuti, taona, cisanu catha,Mvula yapita yaleka;

Werengani mutu wathunthu Nyimbo 2