Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nyimbo 2:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndine duwa lofiira la ku Saroni,Ngakhale kakombo wa kuzigwa.

2. Ngati kakombo pakati pa mingaMomwemo wokondedwa wanga pakati pa ana akazi.

3. Ngati maula pakati pa mitengo ya m'nkhalango,Momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana amuna.Ndinakondwa pakukhala pa mthunzi wace,Zipatso zace zinatsekemera m'kamwa mwanga.

4. Anandifikitsa ku nyumba ya vinyo,Mbendera yace yondizolimira inali cikondi.

Werengani mutu wathunthu Nyimbo 2