22. Ndipo atatero, Alevi analowa kucita Debito yao m'cihema cokomanako pamaso pa Aroni, ndi pamaso pa ana ace amuna; monga Yehova anauza Mose kunena za Alevi, momwemo anawacitira.
23. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
24. Ici ndi ca Alevi: kuyambira ali wa zaka makumi awiri ndi zisanu ndi mphambu azilowa kutumikira utumikiwu mu nchito ya cihema cokomanako;
25. ndipo kuyambira zaka makumi asanu azileka kutumikira utumikiwu, osacitanso nchitoyi;
26. koma atumikire pamodzi ndi abale ao m'cihema cokomanako, kusunga udikirowo, koma osagwira nchito. Utere nao Alevi kunena za udikiro wao.