1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2. Nena kwa Aroni, nuti naye, Pamene uyatsa nyalizo, nyali manu ndi ziwirizo ziwale pandunji pace pa coikapo nyalico.
3. Ndipo Aroni anacita cotero; anayatsa nyalizo kuti ziwale pandunji pace pa coikapo nyali, monga Yehova adauza Mose.
4. Ndipo mapangidwe ace a coikapo nyali ndiwo golidi wosula; kuyambira tsinde lace kufikira maluwa ace anacisula; monga mwa maonekedwe ace Yehova anaonetsa Mose, momwemo anacipanga coikapo nyali.
5. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
6. Uwatenge Alevi pakati pa ana a Israyeli, nuwayeretse.
7. Ndipo utere nao kuwayeretsa: uwawaze madzi akucotsa zoipa, ndipo apititse lumo pa thupi lao lonse, natsuke zobvala zao, nadziyeretse.