Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 8:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2. Nena kwa Aroni, nuti naye, Pamene uyatsa nyalizo, nyali manu ndi ziwirizo ziwale pandunji pace pa coikapo nyalico.

3. Ndipo Aroni anacita cotero; anayatsa nyalizo kuti ziwale pandunji pace pa coikapo nyali, monga Yehova adauza Mose.

4. Ndipo mapangidwe ace a coikapo nyali ndiwo golidi wosula; kuyambira tsinde lace kufikira maluwa ace anacisula; monga mwa maonekedwe ace Yehova anaonetsa Mose, momwemo anacipanga coikapo nyali.

Werengani mutu wathunthu Numeri 8