29. Kunena za ana a Merari, Uwawerenge monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao.
30. Uwawerenge kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kucita nchito ya cihema cokomanako.
31. Ndipo udikiro wa akatundu ao, monga mwa nchito zao zonse m'cihema cokomanako ndi ici: matabwa a kacisi, ndi mitanda yace, ndi mizati ndi nsanamira zace, ndi makamwa ace;
32. ndi nsici za kubwalo kozungulira, ndi makamwa ace, ndi ziciri zace, ndi zingwe zace, pamodzi ndi zipangizo zace zonse, ndi nchito yace yonse; ndipo muziwerenga zipangizo za udikiro wa akatundu ao ndi kuwaehula maina ao.
33. Iyi ndi nchito ya mabanja a ana a Merari, monga mwa nchito zao zonse m'cihema cokomanako, mowauza Itamara mwana wa Aroni wansembe.
34. Ndipo Mose ndi Aroni ndi akalonga a khamu anawerenga ana a Akohati monga mwa mabanja ao, ndi monga mwa nyumba za makolo ao,
35. kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kuti agwire Debito m'cihema cokomanako;
36. ndipo owerengedwa ao monga mwa mabanja ao ndiwo zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu.