Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 4:19-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. koma muzitero nao kuti akhale ndi moyo, osafa ai, poyandikiza iwo zopatulikitsazo; Aroni ndi ana ace amuna alowe, namuikire munthu yense nchito yace ndi katundu wace.

20. Koma asalowe kukaona zopatulikazo pozikulunga, kuti angafe.

21. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

22. Werenganso ana a Gerisoni, monga mwa nyumba za makolo ao, monga mwa mabanja ao.

23. Uwawerenge kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu, kufikira a zaka makumi asanu; onse akulowa kutumikira utumikiwo, kucita nchitoyi m'cihema cokomanako.

24. Nchito ya mabanja a Agerisoni, pogwira nchito ndi kusenza katundu ndi iyi;

25. azinyamula nsaru zophimba za kacisi, ndi cihema cokomanako, cophimba cace, ndi cophimba ca zikopa za akatumbu ciri pamwamba pace, ndi nsaru yotsekera pa khomo la cihema cokomanako;

26. ndi nsaru zocingira za pabwalo, ndi nsaru yotsekera ku cipata ca pabwalo liri pakacisi ndi pa guwa la nsembe pozungulira, ndi zingwe zao, ndi zipangizo zonse za Debito zao, ndi zonse acita nazo; m'menemo muli nchito zao.

27. Nchito yonse ya ana a Agerisoni, kunena za akatundu ao ndi nchito zao zonse, ikhale monga adzanena Aroni ndi ana ace amuna; ndipo muwaike adikire akatundu ao onse.

Werengani mutu wathunthu Numeri 4