Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 4:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo zoyang'anira Eleazara, mwana wa Aroni wansembe, ndizo mafuta a nyaliyo, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsembe yaufa kosalekeza, ndi mafuta odzoza, udikiro wa kacisi wonse, ndi zonse ziri m'mwemo, malo opatulika, ndi zipangizo zace.

17. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Dati,

18. Musamasadza pfuko la mabanja a Kohati kuwacotsa pakati pa Alevi;

19. koma muzitero nao kuti akhale ndi moyo, osafa ai, poyandikiza iwo zopatulikitsazo; Aroni ndi ana ace amuna alowe, namuikire munthu yense nchito yace ndi katundu wace.

20. Koma asalowe kukaona zopatulikazo pozikulunga, kuti angafe.

21. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

Werengani mutu wathunthu Numeri 4