6. Colamulira Yehova za ana akazi a Tselofekadi ndi ici, kuti, Akwatibwe nao amene afuna eni ace; komatu akwatibwe nao a banja la pfuko la makolo ao okha okha.
7. Motero colowa ca ana a Israyeli sicidzamka m'pfuko m'pfuko; popeza ana a Israyeli adzamamatira yense ku colowa ca pfuko la makolo ace.
8. Ndipo mwana wamkazi yense wa mapfuko a ana a Israyeli, wakukhala naco colowa, akwatibwe ndi wina wa banja la pfuko la kholo lace, kuti ana a Israyeli akhale naco yense colowa ca makolo ace.
9. Motero colowa ca ana a Israyeli sicidzamka m'pfuko m'pfuko, pakuti mapfuko a ana a Israyeli adzamamatira lonse ku colowa cace cace.
10. Monga Yehova adalamulira Mose, momwemo ana akazi a Tselofekadi anacita;
11. popeza Mala, Tiriza, ndi Hogila, ndi Milika, ndi Nowa, ana akazi a Tselofekadi, anakwatibwa ndi ana amuna a abale a atate wao.
12. Anakwatibwa mwa mabanja a ana a Manase mwana wa Yosefe; ndipo colowa cao dnakhala m'pfuko la banja la atate wao.
13. Awa ndi malamulo ndi maweruzo, amene Yehova analamulira ana a Israyeli ndi dzanja la Mose m'zidikha za Moabu pa Yordano ku Yeriko.