Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 35:29-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Ndipo izi zikhale kwa inu lemba la ciweruzo mwa mibadwo yanu, m'nyumba zanu zonse.

30. Ali yense wakantha munthu, wakupha munthuyo aziphedwa pakamwa pa mboni; koma mboni ya munthu mmodzi isafikire kuti munthu afe.

31. Musamalandira dipo lakuombola moyo wa iye adapha munthu, naparamula imfa; koma aziphedwa ndithu.

32. Musamalandira dipo lakuombola iye amene adathawira ku mudzi wace wopulumukirako, kuti abwerenso kukhala m'dziko, kufikira atafa wansembe.

33. Ndipo musamaipsa dziko muli m'mwemo; popeza mwazi uipsa dziko; pakuti kulibe kutetezera dziko cifukwa ca mwazi anaukhetsa m'mwemo, koma ndi mwazi wa iye anaukhetsa ndiwo.

34. Usamadetsa dziko ukhala m'mwemo, limene ndikhalitsa pakati pace; popeza Ine Yehova ndikhalitsa pakati pa ana a Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Numeri 35