Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 34:18-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Muwatengenso akalonga, kalonga mmodzi ku pfuko limodzi, agawe dziko likhale colowa cao.

19. Maina a amunawo ndiwo: wa pfuko la Yuda, Kalebi mwana wa Yefune.

20. Wa pfuko la ana a Simeoni, Semuyeli mwana wa Amihudi.

21. Wa pfuko la Benjamini, Elidadi mwana wa Kisiloni.

22. Wa pfuko la ana a Dani, kalonga Buki mwana wa Yogili.

23. Wa ana a Yosefe; wa pfuko la ana a Manase, kalonga Haniyeli mwana wa Efodi.

24. Wa pfuko la ana a Efraimu, kalonga Kemuyeli mwana wa Sipitana.

25. Wa pfuko la ana a Zebuloni, kalonga Elisafana mwana wa Paranaki.

26. Wa pfuko la ana a Isakara, kalonga Palitiyeli mwana wa Azana.

27. Wa pfuko la ana a Aseri, kalonga Ahihudi mwana wa Selomi.

28. Wa pfuko la ana a Nafitali, kalonga Pedaheli mwana wa Amihudi.

29. Iwo ndiwo amene Yehova analamulira agawire ana a Israyeli colowa cao m'dziko la Kanani.

Werengani mutu wathunthu Numeri 34