16. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
17. Maina a amunawo adzakugawirani dziko likhale colowa canu, ndi awa: Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18. Muwatengenso akalonga, kalonga mmodzi ku pfuko limodzi, agawe dziko likhale colowa cao.
19. Maina a amunawo ndiwo: wa pfuko la Yuda, Kalebi mwana wa Yefune.
20. Wa pfuko la ana a Simeoni, Semuyeli mwana wa Amihudi.
21. Wa pfuko la Benjamini, Elidadi mwana wa Kisiloni.
22. Wa pfuko la ana a Dani, kalonga Buki mwana wa Yogili.
23. Wa ana a Yosefe; wa pfuko la ana a Manase, kalonga Haniyeli mwana wa Efodi.
24. Wa pfuko la ana a Efraimu, kalonga Kemuyeli mwana wa Sipitana.
25. Wa pfuko la ana a Zebuloni, kalonga Elisafana mwana wa Paranaki.
26. Wa pfuko la ana a Isakara, kalonga Palitiyeli mwana wa Azana.
27. Wa pfuko la ana a Aseri, kalonga Ahihudi mwana wa Selomi.