Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 34:15-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. mapfuko awiriwa ndi hafu adalandira colowa cao tsidya lija la Yordano ku Yeriko, kum'mawa, koturukira dzuwa.

16. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

17. Maina a amunawo adzakugawirani dziko likhale colowa canu, ndi awa: Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni.

18. Muwatengenso akalonga, kalonga mmodzi ku pfuko limodzi, agawe dziko likhale colowa cao.

19. Maina a amunawo ndiwo: wa pfuko la Yuda, Kalebi mwana wa Yefune.

20. Wa pfuko la ana a Simeoni, Semuyeli mwana wa Amihudi.

21. Wa pfuko la Benjamini, Elidadi mwana wa Kisiloni.

22. Wa pfuko la ana a Dani, kalonga Buki mwana wa Yogili.

23. Wa ana a Yosefe; wa pfuko la ana a Manase, kalonga Haniyeli mwana wa Efodi.

24. Wa pfuko la ana a Efraimu, kalonga Kemuyeli mwana wa Sipitana.

25. Wa pfuko la ana a Zebuloni, kalonga Elisafana mwana wa Paranaki.

26. Wa pfuko la ana a Isakara, kalonga Palitiyeli mwana wa Azana.

Werengani mutu wathunthu Numeri 34