Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 34:13-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo Mose anauza ana a Israyeli, nati, Ili ndi dzikoli mudzalandira ndi kucita maere, limene Yehova analamulira awapatse mapfuko asanu ndi anai ndi hafu;

14. popeza pfuko la ana a Rubeni monga mwa nyumba za makolo ao, ndi pfuko la ana a Gadi monga mwa nyumba za makolo ao, adalandira, ndi pfuko la hafu la Manase lalandira colowa cao;

15. mapfuko awiriwa ndi hafu adalandira colowa cao tsidya lija la Yordano ku Yeriko, kum'mawa, koturukira dzuwa.

16. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

17. Maina a amunawo adzakugawirani dziko likhale colowa canu, ndi awa: Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni.

18. Muwatengenso akalonga, kalonga mmodzi ku pfuko limodzi, agawe dziko likhale colowa cao.

19. Maina a amunawo ndiwo: wa pfuko la Yuda, Kalebi mwana wa Yefune.

20. Wa pfuko la ana a Simeoni, Semuyeli mwana wa Amihudi.

21. Wa pfuko la Benjamini, Elidadi mwana wa Kisiloni.

22. Wa pfuko la ana a Dani, kalonga Buki mwana wa Yogili.

Werengani mutu wathunthu Numeri 34