Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 34:10-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo mudzilembere malire a kum'mawa ocokera ku Hazara Enani kumka ku Sefamu;

11. ndi malire adzatsika ku Sefamu kumka ku Ribala, kum'mawa kwa Ayina; ndipo malire adzatsika, nadzafikira mbali ya nyanja ya Kinereti kum'mawa,

12. ndi malire adzatsika ku Yordano, ndi kuturuka kwace kudzakhala ku Nyanja ya Mcere; ili ndili dziko lanu monga mwa malire ace polizinga.

13. Ndipo Mose anauza ana a Israyeli, nati, Ili ndi dzikoli mudzalandira ndi kucita maere, limene Yehova analamulira awapatse mapfuko asanu ndi anai ndi hafu;

14. popeza pfuko la ana a Rubeni monga mwa nyumba za makolo ao, ndi pfuko la ana a Gadi monga mwa nyumba za makolo ao, adalandira, ndi pfuko la hafu la Manase lalandira colowa cao;

15. mapfuko awiriwa ndi hafu adalandira colowa cao tsidya lija la Yordano ku Yeriko, kum'mawa, koturukira dzuwa.

16. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

17. Maina a amunawo adzakugawirani dziko likhale colowa canu, ndi awa: Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni.

18. Muwatengenso akalonga, kalonga mmodzi ku pfuko limodzi, agawe dziko likhale colowa cao.

19. Maina a amunawo ndiwo: wa pfuko la Yuda, Kalebi mwana wa Yefune.

20. Wa pfuko la ana a Simeoni, Semuyeli mwana wa Amihudi.

21. Wa pfuko la Benjamini, Elidadi mwana wa Kisiloni.

22. Wa pfuko la ana a Dani, kalonga Buki mwana wa Yogili.

23. Wa ana a Yosefe; wa pfuko la ana a Manase, kalonga Haniyeli mwana wa Efodi.

24. Wa pfuko la ana a Efraimu, kalonga Kemuyeli mwana wa Sipitana.

25. Wa pfuko la ana a Zebuloni, kalonga Elisafana mwana wa Paranaki.

Werengani mutu wathunthu Numeri 34