Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 31:44-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

44. ndi ng'ombe zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi cimodzi,

45. ndi aburu zikwi makumi atatu ndi mazana asanu,

46. ndi anthu zikwi khumi ndi zisanu ndi cimodzi,)

47. mwa gawolo la ana a Israyeli Mose anatenga munthu mmodzi mwa makumi asanu, ndi zoweta momwemo, nazipereka kwa Alevi, akusunga udikiro wa kacisi wa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

48. Pamenepo akazembe a pa ankhondo zikwi, atsogoleri a zikwi, ndi atsogoleri a mazana, anayandikiza kwa Mose;

49. nati kwa Mose, Atumiki anu anawerenga ankhondo tinali nao, ndipo sanasowa munthu mmodzi wa ife.

Werengani mutu wathunthu Numeri 31