Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 3:9-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo uzipereka Alevi kwa Aroni ndi kwa ana ace amuna; apatsidwa kwa iye ndithu, ocokera kwa ana a Israyeli.

10. Koma uike Aroni ndi ana ace amuna, azisunga nchito yao ya nsembe; ndi mlendo wakusendera pafupi amuphe.

11. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

12. Ndipo taonani, Ine ndatenga Alevi kuwacotsa pakati pa ana a Israyeli m'malo mwa ana ovamba onse, oyamba kubadwa mwa ana a Israyeli; ndipo Aleviwo ndi anga.

13. Pakuti ana oyamba onse ndi anga; tsiku lija ndinakantha ana oyamba onse m'dziko la Aigupto ndinadzipatulira ana oyamba onse m'Israyeli, kuyambira munthu kufikira coweta; ndiwo anga; Ine ndine Yehova.

14. Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'cipululu ca Sinai, nati,

15. Werenga ana a Levi monga mwa nyumba ya makolo ao, monga mwa mabanja ao; uwawerenge mwamuna yense wa mwezi umodzi ndi mphambu.

16. Ndipo Mose anawawerenga monga mwa mau a Yehova, monga adamuuza.

17. Ndipo ana a Levi maina ao ndi awa: Gerisoni, ndi Kohati ndi Merari.

18. Ndi ana a Gerisoni maina ao ndi awa, monga mwa mabanja ao: Libini, ndi Simei.

19. Ndi ana a Kohati monga mwa mabanja ao: Amiramu ndi lzara, Hebroni ndi Uziyeli.

20. Ndi ana a Merari monga mwa mabanja ao: Mali ndi Musi. Awa ndi mabanja a Alevi monga mwa nyumba za makolo ao.

21. Banja la Libini, ndi mabanja a Simei, ndiwo a Gerisoni; ndiwo mabanja a Gerisoni.

22. Owerengedwa ao, powawerenga amuna onse, kuyambira mwana wa mwezi umodzi ndi mphambu, owerengedwa ao ndiwo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu.

23. Mabanja a Agerisoni azimanga mahema ao pambuyo pa kacisi kumadzulo.

24. Ndipo kalonga wa nyumba ya makolo a Agerisoni ndiye Eliyasafe mwana wa Layeli.

Werengani mutu wathunthu Numeri 3