Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 3:14-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'cipululu ca Sinai, nati,

15. Werenga ana a Levi monga mwa nyumba ya makolo ao, monga mwa mabanja ao; uwawerenge mwamuna yense wa mwezi umodzi ndi mphambu.

16. Ndipo Mose anawawerenga monga mwa mau a Yehova, monga adamuuza.

17. Ndipo ana a Levi maina ao ndi awa: Gerisoni, ndi Kohati ndi Merari.

18. Ndi ana a Gerisoni maina ao ndi awa, monga mwa mabanja ao: Libini, ndi Simei.

19. Ndi ana a Kohati monga mwa mabanja ao: Amiramu ndi lzara, Hebroni ndi Uziyeli.

20. Ndi ana a Merari monga mwa mabanja ao: Mali ndi Musi. Awa ndi mabanja a Alevi monga mwa nyumba za makolo ao.

21. Banja la Libini, ndi mabanja a Simei, ndiwo a Gerisoni; ndiwo mabanja a Gerisoni.

22. Owerengedwa ao, powawerenga amuna onse, kuyambira mwana wa mwezi umodzi ndi mphambu, owerengedwa ao ndiwo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu.

23. Mabanja a Agerisoni azimanga mahema ao pambuyo pa kacisi kumadzulo.

24. Ndipo kalonga wa nyumba ya makolo a Agerisoni ndiye Eliyasafe mwana wa Layeli.

25. Ndipo udikiro wa ana a Gerisoni m'cihema cokomanako ndiwo kacisi, ndi cihema, cophimba cace, ndi nsaru yotsekera pa khomo la cihema cokomanako,

26. ndi nsaru zocinga za kubwalo, ndi nsaru yotsekera pa cipata ca pabwalo, lokhala kukacisi, ndi ku guwa la nsembe pozungulira, ndi zingwe zace za ku nchito zace zonse.

27. Banja la Aamiramu, ndi banja la Aizara, ndi banja la Ahebroni, ndi banja la Auziyeli ndiwo a Kohati; ndiwo mabanja a Akohati.

Werengani mutu wathunthu Numeri 3