Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 29:11-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo, pamodzi ndi nsembe yaucimo yotetezera, ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira.

12. Ndipo tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi wacisanu ndi ciwiri muzikhala nako kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena, koma mucitire Yehova madyerero masiku asanu ndi awiri;

13. ndipo mubwere nayo nsembe yopsereza, ndiyo nsembe yamoto, ya pfungo lokoma kwa Yehova: ng'ombe zamphongo khumi ndi zitatu, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai, a caka cimodzi, akhale opanda cirema;

14. ndi nsembe yace yaufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, atatu a magawo khumi akhale a ng'ombe imodzi, momwemo nazo ng'ombe khumi ndi zitatuzo, awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo imodzi, momwemo nazo nkhosa zamphongo ziwirizo;

15. ndi limodzi la magawo khumi likhale la mwana wa nkhosa mmodzi, momwemo nao ana a nkhosa khumi ndi anai;

16. ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo; pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira.

17. Ndipo tsiku laciwiri muzibwera nazo ng'ombe zamphongo khumi ndi ziwiri, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai a caka cimodzi, opanda cirema;

18. ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira, za ng'ombe, za nkhosa zamphongo, ndi za ana a nkhosa, monga mwa kuwerenga kwace, ndi kutsata lemba lace;

Werengani mutu wathunthu Numeri 29