Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 28:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo nsembe zace zothira ndizo: limodzi la magawo khumi la bini wa vinyo ndiwo wa ng'ombe imodzi, ndi limodzi la magawo atatu la hini likhale la nkhosa yamphongo, ndi limodzi la magawo anai a hini likhale la mwana wa nkhosa; ndiyo nsembe yopsereza ya mwezi uli wonse kunena miyezi yonse ya caka.

15. Ndi tonde mmodzi, akhale nsembe yaucimo ya Yehova; aikonze pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yothira.

16. Ndipo mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi, pali paskha wa Yehova.

17. Ndipo tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi uwu pali madyerero; masiku asanu ndi awiri azidya mkate wopanda cotupitsa.

18. Tsiku loyamba pali kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena;

19. koma mubwere nayo nsembe yamoto, nsembe yopsereza ya Yehova; ng'ombe ziwiri zamphongo, ndi nkhosa yamphongo imodzi, ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi; akhale kwa inu opanda cirema;

20. ndi nsembe yao ya ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta; mupereke atatu a magawo khumi akhale a ng'ombe, ndi awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo;

Werengani mutu wathunthu Numeri 28