Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 28:13-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. ndi limodzi la magawo khumi la ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa, ndiwo wa mwana wa nkhosa yense; ndiyo nsembe yopsereza ya pfungo lokoma, nsembe yamoto ya. Yehova.

14. Ndipo nsembe zace zothira ndizo: limodzi la magawo khumi la bini wa vinyo ndiwo wa ng'ombe imodzi, ndi limodzi la magawo atatu la hini likhale la nkhosa yamphongo, ndi limodzi la magawo anai a hini likhale la mwana wa nkhosa; ndiyo nsembe yopsereza ya mwezi uli wonse kunena miyezi yonse ya caka.

15. Ndi tonde mmodzi, akhale nsembe yaucimo ya Yehova; aikonze pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yothira.

16. Ndipo mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi, pali paskha wa Yehova.

17. Ndipo tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi uwu pali madyerero; masiku asanu ndi awiri azidya mkate wopanda cotupitsa.

18. Tsiku loyamba pali kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena;

19. koma mubwere nayo nsembe yamoto, nsembe yopsereza ya Yehova; ng'ombe ziwiri zamphongo, ndi nkhosa yamphongo imodzi, ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi; akhale kwa inu opanda cirema;

20. ndi nsembe yao ya ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta; mupereke atatu a magawo khumi akhale a ng'ombe, ndi awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo;

21. upereke limodzi la magawo khumi likhale la mwana wa nkhosa mmodzi; uzitero ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri;

22. ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo, yakutetezera inu.

23. Mupereke izi pamodzi ndi nsembe yopsereza ya m'mawa, ndiyo ya nsembe yopsereza kosalekeza.

24. Momwemo mupereke cakudya ca nsembe yamoto ca pfungo lokoma la Yehova, tsiku ndi tsiku, masiku asanu ndi awiri, cakupereka pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yothira.

25. Ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri mukhale nako kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena.

26. Momwemonso tsiku la zipatso zoyamba, pobwera nayo nsembe ya ufa watsopano kwa Yehova, m'madyerero anu a masabata, muzikhala nako kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena.

27. Pamenepo muzipereka nsembe yopsereza ya pfungo lokoma kwa Yehova; ng'ombe zamphongo ziwiri, nkhosa yamphongo imodzi, ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi;

28. ndi nsembe yace ya ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, atatu a magawo khumi akhale a ng'ombe imodzi, awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo imodzi,

29. limodzi la magawo khumi likhale la mwana wa nkhosa mmodzi, momwemo ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri;

Werengani mutu wathunthu Numeri 28