Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 27:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo umuikirepo ulemerero wako, kuti khamu lonse la ana a Israyeli ammvere.

21. Ndipo aime pamaso pa Eleazara wansembe, amene amfunsire monga mwa ciweruzo ca Urimu pamaso pa Yehova; ponena iye azituruka, ndi ponena iye azilowa, ndi iye ndi ana onse a Israyeli pamodzi naye, ndiwo khamu lonse.

22. Ndipo Mose anacita monga Yehova adamuuza; natenga Yoswa namuimitsa pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse;

23. namuikira manja ace, namlangiza monga Yehova adanena ndi dzanja la Mose.

Werengani mutu wathunthu Numeri 27