Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 27:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Utenge Yoswa mwana wa Nuni, ndiye munthu mwa iye muli mzimu, nuike dzanja lako pa iye;

19. numuimike pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse; numlangize pamaso pao.

20. Ndipo umuikirepo ulemerero wako, kuti khamu lonse la ana a Israyeli ammvere.

21. Ndipo aime pamaso pa Eleazara wansembe, amene amfunsire monga mwa ciweruzo ca Urimu pamaso pa Yehova; ponena iye azituruka, ndi ponena iye azilowa, ndi iye ndi ana onse a Israyeli pamodzi naye, ndiwo khamu lonse.

Werengani mutu wathunthu Numeri 27