Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 27:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Kwera m'phiri ili la Abarimu, nupenye dziko limene ndapatsa ana a Israyeli,

13. Utaliona iwenso udzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wako, monga anaitanidwa Aroni mbale wako;

14. popeza munapikisana nao mau anga m'cipululu ca Zini, potsutsana nane khamulo, osandipatula Ine pa madziwo pamaso pao. Ndiwo madzi a Meriba m'Kadesi, m'cipululu ca Zini.

15. Ndipo Mose ananena ndi Yehova, nati,

16. Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, aike munthu pa khamulo,

17. wakuturuka pamaso pao, ndi kulowa pamaso pao, wakuwaturutsa ndi kuwalowetsa; kuti khamu la Ambuye lisakhale ngati nkhosa zopanda mbusa.

18. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Utenge Yoswa mwana wa Nuni, ndiye munthu mwa iye muli mzimu, nuike dzanja lako pa iye;

Werengani mutu wathunthu Numeri 27