10. Ndipo akapanda kukhala nao abale, mupatse abale a atate wace colowa cace.
11. Ndipo akapanda abale a atate wace, mupatse wa cibale cace woyandikizana naye wa pfuko lace colowa cace, likhale lace lace; ndipo likhale kwa ana a Israyeli lemba monga Yehova wamuuza Mose.
12. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Kwera m'phiri ili la Abarimu, nupenye dziko limene ndapatsa ana a Israyeli,
13. Utaliona iwenso udzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wako, monga anaitanidwa Aroni mbale wako;
14. popeza munapikisana nao mau anga m'cipululu ca Zini, potsutsana nane khamulo, osandipatula Ine pa madziwo pamaso pao. Ndiwo madzi a Meriba m'Kadesi, m'cipululu ca Zini.
15. Ndipo Mose ananena ndi Yehova, nati,