Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 26:21-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo ana a Perezi ndiwo: Hezeroni, ndiye kholo la banja la Ahezeroni; Hamuli, ndiye kholo la banja la Ahamuli.

22. Iwo ndiwo mabanja a Yuda monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu zisanu ndi cimodzi kudza mazana asanu.

23. Ana amuna a Isakara monga mwa mabanja ao ndiwo: Tola, ndiye kholo la banja la Atola; Puva, ndiye kholo la banja la Apuni;

24. Yasubi, ndiye kholo la banja la Ayasubi; Simironi, ndiye kholo la banja la Asimironi.

25. Iwo ndiwo mabanja a Isakara monga mwa owerengedwa ao; zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu zinai kudza mazana atatu.

26. Ana amuna a Zebuloni monga mwa mabanja ao ndiwo: Seredi, ndiye kholo la banja la Aseredi; Eloni, ndiye kholo la banja la Aeloni; Yahaliyeli, ndiye kholo la banja la Ayahaliyeli.

27. Iwo ndiwo mabanja a Zebuloni monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu mazana asanu.

28. Ana amuna a Yosefe monga mwa mabanja ao ndiwo: Manase ndi Efraimu.

29. Ana a Manase ndiwo: Makiri, ndiye kholo la banja la Amakiri; ndipo Makiri anabala Gileadi; ndiye kholo la banja la Agileadi,

Werengani mutu wathunthu Numeri 26