Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 23:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Pakuti, pokhala pamwamba pa matanthwe ndimpenya,Pokhala pa zitunda ndimuyang'ana;Taonani, ndiwo anthu akukhala paokha.Osadziwerengera pakati pa amitundu ena,

10. Adzawerenga ndani pfumbi la Yakobo,Kapena kuwerenga limodzi la magawo anai la Israyeli?Ndipo ine ndife monga amafa aongoka mtima,Citsiriziro canga cifanane naco cace!

11. Pamenepo Balaki anati kwa Balamu, Wandicitiranji? Ndinakutenga utemberere adani anga, ndipo taona, wawadalitsa ndithu.

12. Ndipo anayankha nati, Cimene aciika m'kamwa mwanga Yehova, sindiyenera kodi kunena ici?

13. Ndipo Balaki anati naye, Tiyetu, upite nane kumalo kwina, kumene ukawaona; udzaona malekezero ao okha, osawaona onse; ndipo pokhala pamenepo ukanditembererere iwo.

14. Ndipo anamuka naye ku thengo la Zofimu, pamwamba pa Pisiga, namangako maguwa a nsembe asanu ndi awiri, napereka ng'ombe ndi nkhosa pa guwa la nsembe liri lonse.

Werengani mutu wathunthu Numeri 23