1. Ndipo ana a Israyeli anayenda ulendo, namanga mahema m'zigwa za Moabu, tsidya la Yordano ku Yeriko.
2. Ndipo Balaki mwana wa Zipori anaona zonse Israyeli anacitira Aamori.
3. Ndipo Moabu anacita mantha akuru ndi anthuwo, popeza anacuruka; nada mtima Moabu cifukwa ca ana a Israyeli.