Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 21:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo Israyeli anamkantha ndi lupanga lakuthwa, nalanda dziko lace likhale lao lao, kuyambira Arinoni kufikira Yaboki, kufikira ana ai Amoni; popeza malire a ana a Amoni ndiwo olimba.

25. Ndipo Israyeli analanda midzi iyi yonse; nakhala Israyeli m'midzi yonse ya Aamori; m'Hesiboni ndi miraga yace yonse.

26. Popeza Hesiboni ndiwo mudzi wa Sihoni mfumu ya Aamori, imene idathira nkhondo pa mfumu idafayo ya Moabu, nilanda dziko lace m'dzanja lace kufikira Arinoni.

27. Cifukwa cace iwo akunena mophiphiritsa akuti,Idzani ku Hesiboni,Mudzi wa Sihoni umangike, nukhazikike:

28. Popeza moto unaturuka m'Hesiboni,Cirangali ca mota m'mudzi wa Sihoni;Catha Ari wa Moabu,Eni misanje ya Arinoni.

29. Tsoka kwa iwe, Moabu!Mwaonongeka, anthu a Kemosi inu,Anapereka ana ace amuna opulumuka,Ndi ana ace akazi akhale ansinga,Kwa Sihoni mfumu ya Aamori.

Werengani mutu wathunthu Numeri 21