Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 21:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene Mkanani, mfumu ya Aradi, wokhala kumwela, anamva kuti Israyeli anadzera njira ya azondi, anathira nkhondo pa Israyeli, nagwira ena akhale ansinga.

2. Ndipo Israyeli analonjeza cowinda kwa Yehova, nati, Mukadzaperekatu anthu awa m'dzanja langa, ndidzaononga midzi yao konse.

3. Ndipo Yehova anamvera mau a Israyeli, napereka Akanani; ndipo anawaononga konse ndi midzi yao yomwe; nacha dzina lace la malowo Horima.

4. Ndipo anayenda ulendo kucokera ku phiri la Hori, nadzera njira ya Nyanja Yofiira, kupaza ku dziko la Edomu; ndi mtima wa anthu unada cifukwa ca njirayo.

5. Ndipo anthu ananena motsutsana ndi Mulungu, ndi Mose, ndi kuti, Mwatikwezeranji kuticotsa ku Aigupto kuti tifere m'cipululu? pakuti mkate ndi madzi palibe, ndi mtima wathu walema nao mkate wacabe uwu.

Werengani mutu wathunthu Numeri 21