Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 20:22-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo anayenda ulendo kucokera ku Kadesi; ndi ana a Israyeli, ndilo khamu lonse, anadza ku phiri la Hori.

23. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni m'phiri la Hori, pa malire a dziko la Edomu, ndi kuti,

24. Aroni adzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wace; pakuti sadzalowa m'dziko limene ndapatsa ana a Israyeli, popeza munapikisana ndi mau anga ku madzi a Meriba.

25. Tenga Aroni ndi Eleazara mwana wace, nukwere nao m'phiri la Hori;

26. nubvule Aroni zobvala zace, numbveke Eleazara mwana wace; ndipo Aroni adzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wace, nadzafa komweko.

Werengani mutu wathunthu Numeri 20