Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 17:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2. Nena ndi ana a Israyeli, nulandire kwa yense ndodo, banja liri onse la makolo ndodo imodzi, mafuko ao onse monga mwa mabanja a makolo ao azipereka ndodo, zikhale khumi ndi ziwiri; nulembe dzina la yense pa ndodo yace.

3. Ndipo ulembe dzina la Aroni pa ndodo ya Levi; pakuti pakhale ndodo imodzi pa mkuru yense wa nyumba za makolo ao.

4. Ndipo uziike m'cihema cokomanako, cakuno ca mboni, kumene ndikomana ndi inu.

5. Ndipo kudzali, kuti ndodo ya munthu ndimsankheyo, idzaphuka; ndipo ndidzadziletsera madandaulo a ana a Israyeli amene adandaula nao pa inu.

6. Ndipo Mose ananena ndi ana a Israyeli, ndipo akalonga ao onse anapereka, yense ndodo imodzi, monga mwa mabanja a makolo ao, ndodo khumi ndi ziwiri; ndi ndodo ya Aroni inakhala pakati pa ndodo zao.

Werengani mutu wathunthu Numeri 17