Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 16:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. kodi muciyesa cinthu cacing'ono, kuti Mulungu wa Israyeli anakusiyanitsani ku khamu la Israyeli, kukusendezani pafupi pa iye, kucita nchito ya kacisi wa Yehova, ndi kuima pamaso pa khamu kuwatumikira;

10. ndi kuti anakusendeza iwe, ndi abale ako onse, ana a Levi, pamodzi ndi iwe? ndipo kodi mufunanso nchito ya nsembe?

11. Cifukwa cace, iwe ndi khamu lonse mwasonkhana kutsutsana ndi Yehova; ndipo Aroniyo ndani, kuti mudandaule pa iye?

12. Ndipo Mose anatuma kukaitaniza Datani ndi Abiramu, ana a Eliyabu; koma anati, Sitifikako:

13. kodi ndi cinthu cacing'ono kuti watikweza kuticotsa m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi, kutipha m'cipululu; koma udziyesanso ndithu kalonga wa ife?

Werengani mutu wathunthu Numeri 16