Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 16:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Citani ici; dzitengereni mbale za zofukiza, Kora, ndi khamu lace lonse;

7. nimuikemo moto, muikenso cofukiza pamenepo, pamaso pa Yehova, mawa; ndipo kudzali kuti amene Yehova amsankha, wopatulika ndiye; mwakula mphamvu, inu ana a Levi.

8. Ndipo Mose ananena ndi Kora, Tamvani tsono, inu ana a Levi;

9. kodi muciyesa cinthu cacing'ono, kuti Mulungu wa Israyeli anakusiyanitsani ku khamu la Israyeli, kukusendezani pafupi pa iye, kucita nchito ya kacisi wa Yehova, ndi kuima pamaso pa khamu kuwatumikira;

10. ndi kuti anakusendeza iwe, ndi abale ako onse, ana a Levi, pamodzi ndi iwe? ndipo kodi mufunanso nchito ya nsembe?

11. Cifukwa cace, iwe ndi khamu lonse mwasonkhana kutsutsana ndi Yehova; ndipo Aroniyo ndani, kuti mudandaule pa iye?

Werengani mutu wathunthu Numeri 16