Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 16:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndiponso sunatilowetsa m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi, kapena kutipatsa colowa ca minda, ndi minda yamphesa; kodi udzakolowola amuna awa maso ao? Sitifikako.

15. Pamenepo Mose adapsa mtima, ndipo anati kwa Yehova, Musasamalira copereka cao; siodinalanda buru wao mmodzi, kapena kucitira coipa mmodzi wa iwowa.

16. Ndipo Mose anati kwa Kora, Iwe ndi khamu lako lonse mukhale pamaso pa Yehova mawa, iwe ndi iwowa, ndi Aroni;

17. nimutenge munthu yense mbale yace yofukizamo, nimuike cofukiza m'mwemo, nimubwere nazo, yense mbale yace yofukizamo pamaso pa Yehova, mbale zofukizamo mazana awiri ndi makumi asanu; ndi iwe, ndi Aroni, yense mbale yace yofukizamo.

Werengani mutu wathunthu Numeri 16