Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 15:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose nati,

2. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mukakalowa m'dziko lokakhalamo inu, limene ndirikupatsa inu,

3. ndipo mukakonzera Yehova nsembe yamoto, nsembe yopsereza, kapena yophera, pocita cowinda ca padera, kapena nsembe yaufulu, kapena nsembe ya pa nyengo zanu zoikika, kumcitira Yehova pfungo lokoma, la ng'ombe kapena nkhosa;

4. pamenepo iye wobwera naco copereka cace kwa Yehova, azibwera nayo nsembe yaufa, limodzi la magawo khumi la ufa wosalala, wosanganiza ndi limodzi la magawo anai la bini la mafuta;

Werengani mutu wathunthu Numeri 15