Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 13:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2. Udzitumire amuna, kuti azonde dziko la Kanani, limene ndirikupatsa ana a Israyeli; utumize munthu mmodzi wa pfuko liri lonse la makolo ao, yense kalonga pakati pa anzace.

3. Ndipo Mose anawatumiza kucokera ku cipululu ca Parana monga mwa mau a Yehova; amuna onsewa ndiwo akuru a ana a Israyeli.

4. Maina ao ndi awa: wa pfuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri.

5. Wa pfuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori.

6. Wa pfuko la Yuda, Kalebi mwana wa Yefune.

Werengani mutu wathunthu Numeri 13