Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 13:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2. Udzitumire amuna, kuti azonde dziko la Kanani, limene ndirikupatsa ana a Israyeli; utumize munthu mmodzi wa pfuko liri lonse la makolo ao, yense kalonga pakati pa anzace.

3. Ndipo Mose anawatumiza kucokera ku cipululu ca Parana monga mwa mau a Yehova; amuna onsewa ndiwo akuru a ana a Israyeli.

4. Maina ao ndi awa: wa pfuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri.

5. Wa pfuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori.

6. Wa pfuko la Yuda, Kalebi mwana wa Yefune.

7. Wa pfuko la Isakara, Igali mwana wa Yosefe.

8. Wa pfuko la Efraimu, Hoseya mwana wa Nuni.

9. Wa pfuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu.

10. Wa pfuko la Zebuloni, Gadiyeli mwana wa Sodi.

11. Wa pfuko la Yosefe, wa pfuko la Manase, Gadi mwana wa Susi.

Werengani mutu wathunthu Numeri 13