Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 11:27-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndipo anathamanga anyamata, nauza Mose, nati, Elidadi ndi Medadi alikunenera m'cigono.

28. Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wace, anayankha nati, Mose, mfumu yanga, aletseni.

29. Koma Mose anati kwa iye, Kodi ucita nsanje nao cifukwa ca ine? Mwenzi anthu onse a Yehova atakhala aneneri! mwenzi Yehova atawaikira mzimu wace!

30. Ndipo Mose ndi akulu onse a Israyeli anasonkhana kucigono.

Werengani mutu wathunthu Numeri 11