Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 11:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anthu anaipa, namadandaula m'makutu a Yehova; ndipo pamene Yehova anamva anapsa mtima; ndi mota wa Yehova unayaka pakati pao, nunyeketsa ku cilekezero ca cigono.

2. Pamenepo anthu anapfuulira kwa Mose; ndi Mose anapemphera kwa Yehova, ndi motowo unazimika.

3. Ndipo anacha malowo dzina lace Tabera; popeza moto wa Yehova udayaka pakati pao.

4. Ndipo anthu osokonezeka ali pakati pao anagwidwa naco cilakolako; ndi ana a Israyeli omwe analiranso, nati, Adzatipatsa nyama ndani?

5. Tikumbukira nsomba tinazidya m'Aigupto cabe, mankaka, ndi mavwendi, ndi anyesi a mitundu itatu;

6. koma tsopano moyo wathu waphwa; tiribe kanthu pamaso pathu koma mana awa.

7. Ndipo mana ananga zipatso zampasa, ndi maonekedwe ace ngati maonekedwe a bedola.

Werengani mutu wathunthu Numeri 11