Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 11:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anthu anaipa, namadandaula m'makutu a Yehova; ndipo pamene Yehova anamva anapsa mtima; ndi mota wa Yehova unayaka pakati pao, nunyeketsa ku cilekezero ca cigono.

2. Pamenepo anthu anapfuulira kwa Mose; ndi Mose anapemphera kwa Yehova, ndi motowo unazimika.

3. Ndipo anacha malowo dzina lace Tabera; popeza moto wa Yehova udayaka pakati pao.

4. Ndipo anthu osokonezeka ali pakati pao anagwidwa naco cilakolako; ndi ana a Israyeli omwe analiranso, nati, Adzatipatsa nyama ndani?

5. Tikumbukira nsomba tinazidya m'Aigupto cabe, mankaka, ndi mavwendi, ndi anyesi a mitundu itatu;

6. koma tsopano moyo wathu waphwa; tiribe kanthu pamaso pathu koma mana awa.

7. Ndipo mana ananga zipatso zampasa, ndi maonekedwe ace ngati maonekedwe a bedola.

8. Anthu amamka, nawaola, nawapera ndi mphero, kapena kuwasinja mumtondo, nawaphika m'mphika, nawaumba timitanda; ndi powalawa anali ngati timitanda tokazinga ndi mafuta.

9. Ndipo pakugwa mame pacigono usiku, mana anagwapo.

10. Ndipo Mose anamva anthu alikulira m'mabanja ao, yense pakhomo pa hema wace; ndipo Yehova anapsa mtima ndithu, ndipo kudamuipira Mose.

11. Ndipo Mose anati kwa Yehova, Munacitiranji coipa mtumiki wanu? ndalekeranii kupeza ufulu pamaso panu, kuti muika pa ine katundu wa anthu awa onse?

Werengani mutu wathunthu Numeri 11