Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 10:32-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Ndipo kudzatero, ukamuka nafe, inde, kudzali kuti zokoma ziri zonse Yehova aticitira ife, zomwezo tidzakucitira iwe.

33. Ndipo anayenda kucokera ku phiri la Yehova ulendo wa masiku atatu; ndipo likasa la cipangano ca Yehova, linawatsogolera ulendo wa masiku atatu kuwafunira popumulira.

34. Ndipo mtambo wa Yehova unali pamwamba pao msana, pakuyenda iwo kucokera kucigono.

35. Ndipo kunali pakucoka kumka nalo likasa, Mose anati, Ukani Yehova, abalalike adani anu; akuda Inu athawe pamaso panu.

36. Ndi pakupumula ili anati, Bwerani Yehova kwa zikwi zikwi za Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Numeri 10