Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 10:23-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Manase anayang'anira Gamaliyeli mwana wa Pedazuri.

24. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Benjamini anayang'anira Abidana mwana wa Gideoni.

25. Pamenepo anayenda a mbendera ya cigono ca ana a Dani, ndiwo a m'mbuyombuyo a zigono zonse, monga mwa magulu ao; ndi pa gulu lace anayang'anira Ahiyezeri mwana wa Amisadai.

26. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Aseri anayang'anira Pagiyeli mwana wa Okirani.

27. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Nafitali anayang'anira Ahira mwana wa Enani.

28. Potero maulendo a ana a Israyeli anakhala monga mwa magulu ao; nayenda ulendowao.

29. Ndipo Mose anati kwa Hobabu mwana wa Reueli Mmidyani mpongozi wa Mose, Ife tirikuyenda kumka ku malo amene Yehova anati, Ndidzakupatsani awa; umuke nafe, tidzakucitira zokoma; popeza Yehova wanenera Israyeli zokoma.

30. Koma anati kwa iye, Sindidzamuka nanu; koma ndipita ku dziko langa, ndi kwa abale anga.

31. Koma anati, Usatisiyetu; popeza udziwa poyenera kumanga ife m'cipululu, ndipo udzakhala maso athu.

Werengani mutu wathunthu Numeri 10