Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 9:36-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Tapenyani, ife lero ndife akapolo, ndi dzikoli mudalipereka kwa makolo athu kudya zipatso zace ndi zokoma zace, taonani, ife ndife akapolo m'menemo.

37. Ndipo licurukitsira mafumu zipatso zace, ndiwo amene munawaika atiweruze, cifukwa ca zoipa zathu; acitanso ufumu pa matupi athu, ndi pa zaweta zathu, monga umo akonda; ndipo ife tisauka kwakukuru.

38. Ndipo mwa ici conse ticita pangano lokhazikika, ndi kulilemba, ndi akulu athu, Alevi athu, ndi ansembe athu, alikomera cizindikilo.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 9