Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 7:30-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Amuna a ku Rama ndi Geba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.

31. Amuna a ku Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.

32. Amuna a ku Betele ndi Ai, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.

33. Amuna a ku Nebo winayo, makumi asanu kudza awiri.

34. Ana a Elamu winayo, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.

35. Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.

36. Ana a Yeriko, mazana atatu mphambu makumi anai kudza asanu.

37. Ana a Lodi, Hadidi, ndi Ono, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi awiri kudza mmodzi.

38. Ana a Senaa, zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi anai kudza makumi atatu.

39. Ansembe: ana a Yedaya, a nyumba ya Yesuwa, mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu ndi awiri kudza atatu.

40. Ana a Imeri, cikwi cimodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.

41. Ana a Pasuru, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi anai ndi asanu ndi awiri.

42. Ana a Harimu, cikwi cimodzi mphambu khumi limodzi kudza asanu ndi awiri.

43. A Levi: ana a Yesuwa, a Kadimiyeli, a ana a Hodeva, makumi asanu ndi awiri kudza anai.

44. Oyimbira: ana a Asafu, zana limodzi mphambu makumi anai kudza asanu ndi atatu.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 7