30. Amuna a ku Rama ndi Geba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.
31. Amuna a ku Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.
32. Amuna a ku Betele ndi Ai, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.
33. Amuna a ku Nebo winayo, makumi asanu kudza awiri.
34. Ana a Elamu winayo, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.
35. Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.
36. Ana a Yeriko, mazana atatu mphambu makumi anai kudza asanu.
37. Ana a Lodi, Hadidi, ndi Ono, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi awiri kudza mmodzi.
38. Ana a Senaa, zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi anai kudza makumi atatu.
39. Ansembe: ana a Yedaya, a nyumba ya Yesuwa, mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu ndi awiri kudza atatu.
40. Ana a Imeri, cikwi cimodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.
41. Ana a Pasuru, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi anai ndi asanu ndi awiri.
42. Ana a Harimu, cikwi cimodzi mphambu khumi limodzi kudza asanu ndi awiri.
43. A Levi: ana a Yesuwa, a Kadimiyeli, a ana a Hodeva, makumi asanu ndi awiri kudza anai.
44. Oyimbira: ana a Asafu, zana limodzi mphambu makumi anai kudza asanu ndi atatu.